Friday, October 7, 2011

Siwa la pa Utatavu -- Kukumbukira a Steve Jobs

Lero thambo lagwera kopsuta zonse ndipo ng'anga za kompsuta  ndi anthu osiyanasiyana pa dziko lonse ali okhudzidwa ndi kumwalira kwa, bambo Steve Paul Jobs, mmodzi mwa anthu amene anasintha mapangidwe a kompsuta kuyambira pakati pa 1970 kufika chaka chino cha 2011.  A Steve Jobs anatisiya pa 5 Octobala 2011 atavutika  kwa nthawi yayitali ndi mthenda ya khansa ya mu mphafa.

Siwa - Apple.com
 Bambo Steve Paul Jobs anabadwa pa 24 Febuluwale 1955 kwa mwana wa sukulu ya ukachenjede, Joanne Carole Schieble wa ku Amereka. Bambo wake wenieni wa Steve anali Abdulfattah "John" Jandali wa ku Syria.  Abdulfattah ndi  Joanne anapatsana pathupi ali pa sukulu ndiye poona kuti sakanatha kusamala mwanayo, anaganiza zompereka kwa ena kuti amlere. Linali khumbo la amake kuti amtenge anthu okhawo amene anapita ku sukulu za ukachenjede kuti mwanayonso adzapite kusukulu ya ukachenjede.

Pa nthawiyi, panali  anthu angapo amene anawonetsa chidwi ndipo anapikitsana kumchita mayere kuti amtenge mwanayo akabadwa. Makolo amene amamufuna mwana kwambiri anali bambo amene amagwira ntchito yoyimira anthu pa milandu ndi mkazi wawo, koma chifukwa choti anmafuna wamkazi anakana kutenga Steve. Kenako bambo Paul Jobs ndi mkazi wawo, Clara, amane anali asanapiteko ku sukulu ya ukachenjede, anadzipereka kuti amsamalira mwanayo koma atalumbira kuti mwanayo adzampititsa ku sukulu ya ukachenjede monga mmene anafunira mayi wake Joanne.

Steve Jobs ali ndi zaka 17 anapita kusukulu ya ukachenjede ya Reed, yomwe pa nthawiyo inali yodula zedi. Ndalama za makolo ake, a Paul and Clara Jobs, zimathera kulipira sukulu ya mwanayo. Koma Steve anaganiza zoyisiya sukulu chifuwa samaona phindu lake. Sankaziwa kuti adzapanganji mmoyo komanso nanga sukulu idzamthandizanji.

Steve Jobs atasiya sukulu, anayamba kugwira ntchito pa kampani ya Atari, yomwe imapanga masewero a pa kanema. Koma mchaka cha 1976, Steve ndi anzake ena awiri, Steve Wozniak komanso Ronald Wayne, anayambitsa kampani yawo yopanga kompsuta, ya Apple. Wozniak anali mnzake kwambiri wa Steve Jobs kuyambira mu chaka cha 1976, ndiye amakonda kwabasi.. Iwo anasankha apulozi kukhala chizindikiro cha kampani yawo.
Ntchito za manja awo, a Steve Jobs, zikuchitira umboni -- Wojambula Johnathan Mak
Kampani ya Apple inali imodzi mwa kampani zimene mchaka cha 1984 zinayambitsa kupanga kopsuta za mazenera, posiyana ndi kopsuta zomwe zimagwiritsa ntchito mgwindiro (command line interface). Mmenemo mkuti kampani ya Microsoft isanatulukire ukadaulo wa mazenerawu. Kompsuta zawo zoyambirira zimatchedwanso Apple, koma mchaka cha 1984cho anapanga mtundu wina wa kompsuta ndi kuutcha Macintosh. Makono, Macintosh inavinidwa ndipo imangodziwika ndi dzina loti Mac.

Lero, tikamaona nkhani pa utatavu, zolukidwa bwino mwaluso, zokhala ndi thendo la zithunzi pena makanema, linali loto la Steve kuti kompsuta ikhale yosavuta kuyigwiritsa ntchito. Mpaka la lero, Mac ndi kompsuta zochititsa kaso. Kupatula kopsuta, kampani ya Apple yatulutsa lamya za iPhone, gumbagumba za mmanja za iPod, ndi masileti onga kompsuta a iPad mwa zina. Mayina a zinthu zmabiri za ku Apple amayamba ndi "i", monga iMac, iPhone, iPod, iPad, ndi iTunes, mpaka Steve Jobs anapatsidwa ndi dzina la mchezo kuti iSteve.

Kumwalira kwa a Jobs ndi vuto lalikulu chifukwa anali mzati wa kampani ya Apple. Tikampeza kuti mlowam'malo!? Anthu ambiri amene amawadziwa a Steve Jobs akhala akupereka mauthenga opepetsa kubanja lawo komanso kampani ya Apple. Ena mwa anthu wotchuka ndi mtsogoleri wa dziko la Amereka a Barak Obama, mwini kampani ya Microsoft a Bill Gates, mwini  wa chipala cha nkhope (Facebook) a Mark Zuckerberg ndi mzawo wa pamtima a Steve Wozniak.

Pali zambiri zomwe tingathe kukamba za Steve Jobs, koma chifukwa tili pa zovuta, tibaleka kudikira kuti mfumu ikapume kaye. Tidzafotokoza bwino lomwe patsogolo. 

Yaponda thope yamwa!!

No comments:

Post a Comment