Tuesday, January 17, 2012

Chaka Chatsopano kwa Nonse

Ndikulandireni mwapadera abale nonse amene mumakonda kuwerenga nkhani pa bwalo lino. Ndikukhulupirira kuti mwachimaliza bwino chaka cha 2011, ndipo mwayambapo kukwaniritsa ena mwa malingaliro amene muli nawo a mchilumika chino cha 2012.

Chaka cha 2011 chinali chopambana ku chiyankhulo cha Chichewa chifukwa pali zinthu zingapo zimene zinachitika zomwe zakupititsa patsogolo kugwiritsidwa kwa Chichewa pa utatavu ndi m'kopsuta. Mwa zina, mphunzitsi wa sukulu ina ya ukachenjede ku Amereka, a Kelvin Scannell, anatsegula madambwe awiri: http://indigenoustweets.com ndi http://indigenousblogs.com omwe akupititsa patsogolo kugwiritsidwa ntchito kwa ziyankhulo zachimidzimidzi pa utatavupa. http://indigenousblogs.com ndi ndala chabe la indigenoustweets.com/blogs.

Kwa amene sanamvepo za madabwewa, tingonena mopaza. indigenoustweets.com imatolera mitongoliro pa Twitter kaundula wa akadyolidyoli a ziyankhulo zosiyanasiyana. Apapa dzina loti akadyolidyoli silikutanthauza akavuwevuwe osokoneza, koma awa ndi anthu amene amakhala akutumiza timitu tankhani (mitongoliro) pa Twitter kuthandiza enafe kumva zochitika mmaderamu. Momwemo, dambwe la http://indigenousblogs.com limatolera zibaluwa zolembedwa mziyankhulo zimenezi. Dambwe limeneli ndi njira yothandiza kuti mudzitha kupeza nkhani m'ziyakhulo ngati zathuzi mosavuta. Mukudziwa kuti nkhani zambiri pa utatavupa zimakhala m'Chingerezi, m'Chifalaansa ndi ziyankhulo zina zomwe zili ndi mphamvu pa chuma ndi chitukuko. Nkhani za m'Chichewa zimapezeka pa http://indigenousblogs.com/ny (kapenanso ulalo wotanimphirako: http://indigenoustweets.com/blogs/ny). Ndili wokondwa kuti mwa ziyankhulo zina zomwe zilipo, Chichewa chinali chimodzi mwa zoyambirira kuyikidwapo pa m'ndandanda owoneka nawo pa madambwe amenewa.

Mchaka changothachi, ndinakhadzikitsanso dambwe lino lomwe lidzikhala ndi nkhani zosiyanasiyana zokhudza luso la makono monga kompsuta. Kwa ine ndikuona kuti likhala lothandiza poluka mawu atsopano onena zokhudza luso la makono. Kupatula apo, tidzikhalapo ndi nkhani ziwiri pena zitatu za maluso zoti nkuchotsera dalazi m'maso. Kumapeto kwa chakaku, ndinachita nthangwanika zinan'zina monga mukudziwa kuti kumakhala gwiragwira, ndiye ndinangoti du! osalembako kanthu pano. Koma chaka chino ndiyesesa ndithu  kulemba pafupipafupi kuti inunso mudzisangala.

Mchaka cha 2012, ndikuyembekezera zazikulu kuchitika pa nkhani za luso pa Malawi pano. Poti bwamsatsi sawenga mafuta pagulu, sindineneratu kuti kulinji. Koma ndikukhulupirira kuti, mwa zisomo za Chiuta, tabwinotabwino tikhalanso tikutulukira kubwalo. Ndikhulupirira kuti inu musangalala powerenga tikhani ta luso pa dambwe lino.

Zikomo!

No comments:

Post a Comment